Salimo 57
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide, pamene anathawa Sauli kupita ku phanga. 
 1 Mundichitire chifundo, Inu Mulungu mundichitire chifundo, 
pakuti mwa Inu moyo wanga umathawiramo. 
Ndidzathawira mu mthunzi wa mapiko anu 
mpaka chiwonongeko chitapita. 
 2 Ine ndikufuwulira kwa Mulungu Wammwambamwamba, 
kwa Mulungu amene amakwaniritsa cholinga chake pa ine. 
 3 Mulungu amanditumizira kuchokera kumwamba ndi kundipulumutsa, 
kudzudzula iwo amene akundithamangitsa kwambiri. 
Mulungu amatumiza chikondi chake ndi kukhulupirika kwake. 
 4 Ine ndili pakati pa mikango, 
ndagona pakati pa zirombo zolusa; 
anthu amene mano awo ndi milomo yawo ndi mivi, 
malilime awo ndi malupanga akuthwa. 
 5 Mukwezekedwe Inu Mulungu, kuposa mayiko onse akumwamba; 
mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi. 
 6 Iwo anatchera mapazi anga ukonde 
ndipo ndinawerama pansi mosautsidwa. 
Anakumba dzenje mʼnjira yanga 
koma agweramo okha mʼmenemo. 
 7 Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu 
mtima wanga ndi wokhazikika. 
Ndidzayimba nyimbo, nyimbo yake yamatamando. 
 8 Dzuka moyo wanga! 
Dzukani zeze ndi pangwe! 
Ndidzadzuka mʼbandakucha. 
 9 Ndidzakutamandani Ambuye, pakati pa mitundu ya anthu, 
ndidzayimba za Inu pakati pa mayiko. 
 10 Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kufikira ku mayiko akumwamba; 
kukhulupirika kwanu kwafika ku mitambo. 
 11 Mukwezekedwe Inu Mulungu kuposa mayiko akumwamba, 
Languages