Salimo 3
Salimo la Davide. Atathawa mwana wake Abisalomu. 
 1 Inu Yehova, achulukadi adani anga! 
Achulukadi amene andiwukira! 
 2 Ambiri akunena za ine kuti, 
“Mulungu sadzamupulumutsa.” 
Sela
  3 Koma Inu Yehova, ndinu chishango chonditeteza, 
Inu mwandiveka ulemerero ndipo mwanditukula. 
 4 Kwa Yehova, Ine ndilira mofuwula 
ndipo Iye amandiyankha kuchokera ku phiri lake loyera. 
Sela
  5 Ine ndimagona ndi kupeza tulo; 
ndimadzukanso chifukwa Yehova amandichirikiza. 
 6 Sindidzaopa adani anga osawerengeka amene 
abwera kulimbana nane kuchokera ku madera onse. 
 7 Dzukani, Inu Yehova! 
Pulumutseni, Inu Mulungu wanga. 
Akantheni adani anga onse pa msagwada; 
gululani mano a anthu oyipa. 
 8 Chipulumutso chimachokera kwa Yehova. 
Madalitso akhale pa anthu anu. 
Sela
 
Languages