Salimo 2
 1 Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu? 
Akonzekeranji zopanda pake anthu? 
 2 Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo; 
ndipo olamulira asonkhana pamodzi 
kulimbana ndi Ambuye 
ndi wodzozedwa wakeyo. 
 3 Iwo akunena kuti, “Tiyeni timasule magoli awo 
ndipo titaye zingwe zawo.” 
 4 Wokhala mmwamba akuseka; 
Ambuye akuwanyoza iwowo. 
 5 Ndipo iye awadzudzula mu mkwiyo wake 
ndi kuwaopseza mu ukali wake, kunena kuti, 
 6 “Ine ndakhazikitsa mfumu yanga 
pa Ziyoni, phiri langa loyera.”
7 Ine ndidzalengeza zimene Yehova walamula:
Iye anati kwa Ine, “Iwe ndiwe mwana wanga; 
lero Ine ndakhala Atate ako. 
 8 Tandipempha, 
ndipo ndidzachititsa kuti mitundu ya anthu ikhale cholowa chako; 
malekezero a dziko lapansi kuti akhale chuma chako. 
 9 Iweyo udzawalamulira ndi ndodo yaufumu yachitsulo; 
udzawaphwanya zidutswazidutswa ngati zowumba zadothi.” 
 10 Kotero, inu mafumu, chenjerani; 
chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi. 
 11 Tumikirani Yehova mwa mantha 
ndi kukondwerera ulamuliro wake monjenjemera. 
 12 Mpsopsoneni mwanayo kuti angakwiye; 
kuti mungawonongedwe mʼnjira zanu, 
pakuti ukali wake utha kuuka mʼkanthawi kochepa. 
Languages