Salimo 110
Salimo la Davide. 
 1 Yehova akuwuza Mbuye wanga kuti, 
“Khala ku dzanja langa lamanja 
mpaka nditasandutsa adani ako 
kukhala chopondapo mapazi ako.” 
 2 Yehova adzakuza ndodo yamphamvu ya ufumu wako kuchokera mʼZiyoni; 
udzalamulira pakati pa adani ako. 
 3 Ankhondo ako adzakhala odzipereka 
pa tsiku lako la nkhondo. 
Atavala chiyero chaulemerero, 
kuchokera mʼmimba ya mʼbandakucha, 
udzalandira mame a unyamata wako. 
 4 Yehova walumbira 
ndipo sadzasintha maganizo ake: 
“Ndiwe wansembe mpaka muyaya 
monga mwa unsembe wa Melikizedeki.” 
 5 Ambuye ali kudzanja lako lamanja; 
Iye adzaponda mafumu pa tsiku la ukali wake. 
 6 Adzaweruza anthu a mitundu ina, 
adzadzaza dziko lapansi ndi mitembo ndipo adzaphwanya olamulira a pa dziko lonse lapansi. 
 7 Iye adzamwa mu mtsinje wa mʼmbali mwa njira; 
Languages