4 Chifukwa cha kufuwulako maziko a zitseko ndi ziwundo anagwedezeka ndipo mʼNyumba ya Yehova munadzaza utsi.
5 Tsono ine ndinafuwula kuti, “Tsoka langa ine! Ndatayika! Pakuti ndine munthu wapakamwa poyipa, ndipo ndimakhala pakati pa anthu a pakamwa poyipa, ndipo ndi maso anga ndaona mfumu Yehova Wamphamvuzonse.”
6 Pomwepo mmodzi mwa Aserafi aja anawulukira kwa ine ali ndi khala lamoto mʼdzanja lake, khala limene analichotsa ndi mbaniro pa guwa lansembe. 7 Ndipo anandikhudza pakamwa panga ndi khala lamotolo nati, “Taona ndakhudza pa milomo yako ndi khalali; kulakwa kwako kwachotsedwa, machimo ako akhululukidwa.”
8 Kenaka ndinamva mawu a Ambuye akuti, “Kodi ndidzatuma yani? Ndipo ndani adzapite mʼmalo mwathu?”
Ndipo ine ndinati, “Ndilipo. Tumeni!”
9 Yehova anati, “Pita ndipo ukawawuze anthu awa:
“ ‘Kumva muzimva, koma osamvetsetsa;
kupenya muzipenya koma osaona kanthu.’
10 Tsono anthu amenewa uwaphe mtima;
uwagonthetse makutu,
ndipo uwatseke mʼmaso.
Mwina angaone ndi maso awo,
angamve ndi makutu awo,
angamvetse ndi mitima yawo,
kenaka ndi kutembenuka mtima ndi kuchiritsidwa.”
11 Pamenepo ine ndinati, “Zimenezo ndi mpaka liti Inu Ambuye?”
Ndipo Iyeyo anandiyankha kuti,
“Mpaka mizinda itasanduka mabwinja
nʼkusowa wokhalamo,
mpaka nyumba zitasowa anthu okhalamo,
mpaka dziko litasanduka chipululu ndithu,
12 mpaka Yehova atasamutsira aliyense kutali,
dziko nʼkusiyidwa kwathunthu.
13 Ndipo ngakhale chigawo chakhumi cha anthu chitatsala mʼdziko,