40 Ndikweza dzanja langa kumwamba ndi kulumbira kuti,
‘Pali Ine wamoyo wamuyaya,
41 pamene ndidzanola lupanga langa lonyezimira
ndipo dzanja liligwira pakubweretsa chiweruzo,
ndidzabwezera chilango adani anga
ndi kulanga onse odana nane.
42 Mivi yanga idzakhuta magazi awo
pamene lupanga langa lidzawononga mnofu:
magazi a anthu ophedwa ndi ogwidwa ukapolo,
mitu ya atsogoleri a adani.’ ”
43 Kondwerani, inu mitundu yonse ya anthu pamodzi ndi anthu ake,
pakuti Iye adzabwezera chilango anthu amene anapha atumiki ake;
adzabwezera chilango adani ake
ndipo adzakhululukira dziko lake ndi la anthu ake.
44 Mose anabwera ndi Yoswa mwana wa Nuni ndipo anayankhula mawu onsewa mʼnyimbo anthu akumva. 45 Mose atatsiriza kunena mawu onsewa pamtima kwa Aisraeli, 46 iye anawawuza kuti, “Muwasunge bwino mu mtima mwanu, mawu onse amene lero lino ndikukuwuzani kuti mudzawuze ana anu, kuti adzamvere mosamalitsa mawu onse a malamulo amenewa. 47 Mawuwa sikuti ndi mawu achabe kwa inu. Mawuwa ndi moyo wanu. Mukawamvera mudzakhala ndi moyo wautali mʼdziko limene mukukalitenga kukhala lanu mukawoloka Yorodani.”
Mose Adzafera pa Phiri la Nebo
48 Tsiku lomwelo Yehova anawuza Mose kuti, 49 “Pita ku mapiri a ku Abarimu ukakwere pa Phiri la Nebo ku Mowabu, moyangʼanana ndi Yeriko, ndipo ukaone dziko la Kanaani, dziko limene ndikulipereka kwa Aisraeli kukhala lawo. 50 Iwe udzafera pa phiri limenelo ndipo udzapita kumene makolo ako anapita, monga mʼbale wako Aaroni anafera pa phiri la Hori ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake. 51 Chifukwa chake nʼchakuti inu nonse awiri simunakhulupirike kwa Ine pamaso pa Aisraeli pa madzi a Meriba ku Kadesi mʼchipululu cha Zini chifukwa simunandilemekeze kokwanira pakati pa Aisraeli. 52 Choncho udzalionera kutali dziko limene ndikupereka kwa Aisraeli. Sudzalowa mʼdziko limene ndi kulipereka kwa Aisraeli.”